20. Yehova anandibwezera monga mwa cilungamo canga;Anandisudzula monga mwa kusisira kwa manja anga.
21. Pakuti ndasunga njira za Yehova,Ndipo sindinacitira coipa kusiyana ndi Mulungu wanga.
22. Pakuti maweruzo ace onse anali pamaso panga,Ndipo malemba ace sindinawacotsa kwa ine.
23. Ndipo ndinakhala wangwiro ndi iye,Ndipo ndinadzisunga wosacita coipa canga.