5. Alemekeze dzina la Yehova;Popeza analamulira, ndipo zinalengedwa.
6. Anazikhazikanso ku nthawi za nthawi;Anazipatsa cilamulo cosatumphika.
7. Lemekezani Yehova kocokera ku dziko lapansi,Zinsomba inu, ndi malo ozama onse;
8. Moto ndi matalala, cipale cofewa ndi nkhungu;Mphepo ya namondwe, yakucita mau ace;
9. Mapiri ndi zitunda zonse;Mitengo yazipatso ndi yamikungudza yonse:
10. Nyama za kuthengo ndi zoweta zonse;Zokwawa, ndi mbalame zakuuluka;