Masalmo 148:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Alemekeze dzina la Yehova;Popeza analamulira, ndipo zinalengedwa.

6. Anazikhazikanso ku nthawi za nthawi;Anazipatsa cilamulo cosatumphika.

7. Lemekezani Yehova kocokera ku dziko lapansi,Zinsomba inu, ndi malo ozama onse;

8. Moto ndi matalala, cipale cofewa ndi nkhungu;Mphepo ya namondwe, yakucita mau ace;

9. Mapiri ndi zitunda zonse;Mitengo yazipatso ndi yamikungudza yonse:

10. Nyama za kuthengo ndi zoweta zonse;Zokwawa, ndi mbalame zakuuluka;

Masalmo 148