Masalmo 145:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Nchito zanu zonse zidzakuyamikani, Yehova;Ndi okondedwa anu adzakulemekezani.

11. Adzanenera ulemerero wa ufumu wanu,Adzalankhulira mphamvu yanu;

12. Kudziwitsa ana a anthu zamphamvu zace,Ndi ulemerero waukuru wa ufumu wace.

13. Ufumu wanu ndiwo ufumu womka muyaya,Ndi kuweruza kwanu kufikira mibadwo yonse yonse.

14. Yehova agwiriziza onse akugwa,Naongoletsa onse owerama.

Masalmo 145