10. Nchito zanu zonse zidzakuyamikani, Yehova;Ndi okondedwa anu adzakulemekezani.
11. Adzanenera ulemerero wa ufumu wanu,Adzalankhulira mphamvu yanu;
12. Kudziwitsa ana a anthu zamphamvu zace,Ndi ulemerero waukuru wa ufumu wace.
13. Ufumu wanu ndiwo ufumu womka muyaya,Ndi kuweruza kwanu kufikira mibadwo yonse yonse.
14. Yehova agwiriziza onse akugwa,Naongoletsa onse owerama.