Masalmo 145:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu;Ndipo ndidzalemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.

2. Masiku onse ndidzakuyamikani;Ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.

3. Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukuru;Ndi ukulu wace ngwosasanthulika.

Masalmo 145