Masalmo 141:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Akandipanda munthu wolungama ndidzati ncifundo:Akandidzudzula, ndidzakuyesa mafuta a pamutu;Mutu wanga usakane:Pakuti pangakhale posautsidwa iwo ndidzawapempherera.

6. Oweruza ao anagwetseka pambali pa thanthwe;Nadzamva mau anga kuti ndiwo okondweretsa.

7. Mafupa athu amwazika pakamwa pa manda,Monga ngati akumba nanyimphula nthaka yapansi.

8. Pakuti maso anga apenya kwanu, Yehova Ambuye;Ndithawira kwa Inu; musataye moyowanga.

9. Mundisunge ndisagwe mumsampha anandicherawo,Ndisakodwe m'makwekwe a iwo ocita zopanda pace,

Masalmo 141