Masalmo 140:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndilanditseni, Yehova, kwa munthu woipa;Ndisungeni kwa munthu waciwawa;

2. Amene adzipanga zoipa mumtima mwao;Masiku onse amemeza nkhondo.

3. Anola lilime lao ngati njoka;Pansi pa milomo yao pali ululu wa mphiri.

4. Ndilindireni Yehova, ndisalowe m'manja mwa woipa;Ndisungeni kwa munthu waciwawa;Kwa iwo akuti akankhe mapazi anga.

5. Odzikuzaanandichera msampha, nandibisira zingwe;Anacha ukonde m'mphepete mwa njira;Anandichera makwekwe.

Masalmo 140