Masalmo 139:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Pakuti asanafike mau pa lilime langa,Taonani, Yehova, muwadziwa onse.

5. Munandizinga kumbuyo ndi kumaso,Nimunaika dzanja lanu pa ine.

6. Kudziwa ici kundilaka ndi kundidabwiza:Kundikhalira patali, sindifikirako.

7. Ndidzapita kuti kuzembera mzimu wanu?Kapena ndidzathawira kuti kuzembera nkhope yanu?

8. Ndikakwera kumka kumwamba, muli komweko;Kapena ndikadziyalira ku Gehena, taonani, muli komweko.

9. Ndikadzitengera mapiko a mbanda kuca,Ndi kukhala ku malekezero a nyanja;

10. Kungakhale komweko dzanja lanu lidzanditsogolera,Nilidzandigwira dzanja lanu lamanja.

11. Ndipo ndikati, Koma mdima undiphimbe,Ndi kuunika kondizinga kukhale usiku:

Masalmo 139