Masalmo 135:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Pakuti Yehova adzaweruza anthu ace,Koma adzaleka atumiki ace.

15. Mafano a amitundu ndiwo siliva ndi golidi,Nchito ya manja a anthu.

16. Pakamwa ali napo koma osalankhula;Maso ali nao, koma osapenya;

17. Makutu ali nao, koma osamva;Inde, pakamwa pao palibe mpweya.

18. Akuwapanga adzafanana nao;Inde, onse akuwakhulupirira.

19. A nyumba ya Israyeli inu, lemekezani Yehova:A nyumba ya Aroni inu, lemekezani Yehova:

20. A nyumba ya Levi inu, lemekezani Yehova:Inu akuopa Yehova, lemekezani Yehova.

Masalmo 135