Masalmo 132:14-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Pampumulo panga mpano posatha:Pano ndidzakhala; pakuti ndakhumbapo.

15. Ndidzadalitsatu cakudya cace;Aumphawi ace ndidzawakhutitsa ndi mkate.

16. Ndipo ansembe ace ndidzawabveka ndi cipulumutso:Ndi okondedwa ace adzapfuulitsa mokondwera.

17. Apo ndidzaphukitsira Davide nyanga;Ndak onzeraru wodzozedwa wanga nyali.

18. Ndidzawabvekaadani ace ndi manyaziKoma pa iyeyu korona wace adzambveka.

Masalmo 132