Masalmo 119:87-105 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

87. Akadandithera pa dziko lapansi; Koma ine sindinasiya malangizo anu.

88. Mundipatse moyo monga mwa cifundo canu;Ndipo ndidzasamalira mboni ya pakamwa panu,

89. Mau anu aikika kumwamba,Kosatha, Yehova.

90. Cikhulupiriko canu cifikira mibadwo mibadwo;Munakhazikitsa dziko lapansi, ndipo likhalitsa.

91. Kunena za maweruzo anu alimbikira kufikira lero;Pakuti onsewa ndiwo atumiki anu.

92. Cilamulo canu cikadapanda kukhala cikondweretso canga,Ndikadatayika m'kuzunzika kwanga.

93. Sindidzaiwala malangizo anu nthawi zonse;Popeza munandipatsa nao moyo.

94. Ine ndine wanu, ndipulumutseniPakuti ndinafuna malangizo anu.

95. Oipa anandilalira kundiononga;Koma ndizindikira mboni zanu.

96. Ndinapenya malekezero ace a ungwiro wonse;Koma lamulo lanu ndi lotakasuka ndithu.

97. Ha! Ndikondadi cilamulo canu;Ndilingiriramo ine tsiku lonse.

98. Malamulo anu andipatsa nzeru yakuposa adani anga;Pakuti akhala nane cikhalire.

99. Ndiri nayo nzeru yakuposa aphunzitsi anga onse;Pakuti ndilingalira mboni zanu.

100. Ndizindikira koposa okalambaPopeza ndinasunga malangizo anu.

101. Ndinaletsa mapazi anga njira iri yonse yoipa,Kuti ndisamalire mau anu.

102. Sindinapatukana nao maweruzo anu;Pakuti Inu munandiphunzitsa.

103. Mau anu azunadi powalawa ine!Koposa uci m'kamwa mwanga.

104. Malangizo anu andizindikiritsa;Cifukwa cace ndidana nao mayendedwe onse acinyengo,

105. Mau anu ndiwo nyali ya ku mapazi anga,Ndi kuunika kwa panjira panga,

Masalmo 119