Masalmo 119:83-86 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

83. Popeza ndakhala ngati thumba lofukirira;Koma sindiiwala malemba anu.

84. Masiku a mtumiki wanu ndiwo angati?Mudzaweruza liti iwo akundilondola koipa?

85. Odzikuza anandikumbira mbuna,Ndiwo osasamalira cilamulo canu.

86. Malamulo anu onse ngokhulupirika;Andilondola nalo bodza; ndithandizeni.

Masalmo 119