83. Popeza ndakhala ngati thumba lofukirira;Koma sindiiwala malemba anu.
84. Masiku a mtumiki wanu ndiwo angati?Mudzaweruza liti iwo akundilondola koipa?
85. Odzikuza anandikumbira mbuna,Ndiwo osasamalira cilamulo canu.
86. Malamulo anu onse ngokhulupirika;Andilondola nalo bodza; ndithandizeni.