Masalmo 119:72-76 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

72. Cilamulo ca pakamwa panu cindikomeraKoposa golidi ndi siliva zikwi zikwi.

73. Manja anu anandilenga nandiumba;Mundizindikiritse, kuti ndiphunzire malemba anu.

74. Iwo amene akuopani adzandiona ine nadzakondwera;Popeza ndayembekezera mau anu;

75. Ndidziwa kuti maweruzo anu ndiwo olungama, Yehova,Ndi kuti munandizunza ine mokhulupirika.

76. Cifundo canu cikhaletu cakunditonthoza, ndikupemphani,Monga mwa mau anu kwa mtumiki wanu.

Masalmo 119