72. Cilamulo ca pakamwa panu cindikomeraKoposa golidi ndi siliva zikwi zikwi.
73. Manja anu anandilenga nandiumba;Mundizindikiritse, kuti ndiphunzire malemba anu.
74. Iwo amene akuopani adzandiona ine nadzakondwera;Popeza ndayembekezera mau anu;
75. Ndidziwa kuti maweruzo anu ndiwo olungama, Yehova,Ndi kuti munandizunza ine mokhulupirika.
76. Cifundo canu cikhaletu cakunditonthoza, ndikupemphani,Monga mwa mau anu kwa mtumiki wanu.