Masalmo 119:7-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndidzakuyanrikani ndi mtima woongoka,Pakuphunzira maweruzo anu olungama.

8. Ndidzasamalira malemba anu:Musandisiye ndithu.

9. Mnyamata adzayeretsa mayendedwe ace bwanji?Akawasamalira monga mwa mau anu.

10. Ndinakufunani ndi mtima wanga wonse;Ndisasokere kusiyana nao malamulo anu.

11. Ndinawabisa mau anu mumtima mwanga,Kuti ndisalakwire Inu.

12. Inu ndinu wodala Yehova;Ndiphunzitseni malemba anu.

13. Ndinafotokozera ndi milomo yangaMaweruzo onse a pakamwa panu,

14. Ndinakondwera m'njira ya mboni zanu,Koposa ndi cuma conse,

15. Ndidzalingirira pa malangizo anu,Ndi kupenyerera mayendedwe anu.

16. Ndidzadzikondweretsa nao malemba anu;Sindidzaiwala mau anu,

17. Mucitire cokoma mtumiki wanu kuti ndikhale ndi moyo;Ndipo ndidzasamalira mau anu.

18. Munditsegulire maso, kuti ndipenyeZodabwiza za m'cilamulo canu.

Masalmo 119