Masalmo 119:68-75 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

68. Inu ndinu wabwino, ndi wakucita zabwino;Mundiphunzitse malemba anu.

69. Odzikuza anandipangira bodza:Ndidzasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.

70. Mtima wao unona ngati mafuta;Koma ine ndikondwera naco cilamulo canu.

71. Kundikomera kuti ndinazunzidwa;Kuti ndiphunzire malemba anu.

72. Cilamulo ca pakamwa panu cindikomeraKoposa golidi ndi siliva zikwi zikwi.

73. Manja anu anandilenga nandiumba;Mundizindikiritse, kuti ndiphunzire malemba anu.

74. Iwo amene akuopani adzandiona ine nadzakondwera;Popeza ndayembekezera mau anu;

75. Ndidziwa kuti maweruzo anu ndiwo olungama, Yehova,Ndi kuti munandizunza ine mokhulupirika.

Masalmo 119