Masalmo 119:63-69 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

63. Ine ndine wakuyanjana nao onse akukuopani,Ndi iwo akusamalira malangizo anu.

64. Dziko lapansi lidzala naco cifundo canu, Yehova;Mundiphunzitse malemba anu.

65. Munacitira mtumiki wanu cokoma, Yehova,Monga mwa mau anu.

66. Mundiphunzitse cisiyanitso ndi nzeru;Pakuti ndinakhulupirira malamulo anu.

67. Ndisanazunzidwe ndinasokera; Koma tsopano ndisamalira mau anu.

68. Inu ndinu wabwino, ndi wakucita zabwino;Mundiphunzitse malemba anu.

69. Odzikuza anandipangira bodza:Ndidzasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.

Masalmo 119