Masalmo 119:53-58 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

53. Ndinasumwa kwakukuru,Cifukwa ca oipa akusiya cilamulo canu.

54. Malemba anu anakhala nyimbo zangaM'nyumba ya ulendo wanga,

55. Usiku ndinakumbukila dzina lanu, Yehova,Ndipo ndinasamalira cilamulo canu.

56. Ici ndinali naco,Popeza ndinasunga malangizo anu.

57. Yehova ndiye gawo langa:Ndinati ndidzasunga mau anu.

58. Ndinapemba pankhope panu ndi mtima wanga wonse:Mundicitire cifundo monga mwa mau anu.

Masalmo 119