Masalmo 119:51-56 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

51. Odzikuza anandinyoza kwambiri:Koma sindinapatukanso naco cilamulo canu.

52. Ndinakumbukila maweruzo anu kuyambira kale, Yehova,Ndipo ndinadzitonthoza.

53. Ndinasumwa kwakukuru,Cifukwa ca oipa akusiya cilamulo canu.

54. Malemba anu anakhala nyimbo zangaM'nyumba ya ulendo wanga,

55. Usiku ndinakumbukila dzina lanu, Yehova,Ndipo ndinasamalira cilamulo canu.

56. Ici ndinali naco,Popeza ndinasunga malangizo anu.

Masalmo 119