5. Ha! mwenzi zitakhazikika njira zangaKuti ndisamalire malemba anu.
6. Pamenepo sindidzacita manyazi,Pakupenyerera malamulo anu onse.
7. Ndidzakuyanrikani ndi mtima woongoka,Pakuphunzira maweruzo anu olungama.
8. Ndidzasamalira malemba anu:Musandisiye ndithu.
9. Mnyamata adzayeretsa mayendedwe ace bwanji?Akawasamalira monga mwa mau anu.
10. Ndinakufunani ndi mtima wanga wonse;Ndisasokere kusiyana nao malamulo anu.
11. Ndinawabisa mau anu mumtima mwanga,Kuti ndisalakwire Inu.