Masalmo 119:23-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Nduna zomwe zinakhala zondineneza;Koma mtumiki wanu analingirira malemba anu.

24. Mboni zanu zomwe ndizo zondikondwetsa,Ndizo zondipangira nzeru.

25. Moyo wanga umamatika ndi pfumbi;Mundipatse moyo monga mwa mau anu.

26. Ndinafotokozera njira zanga, ndipo munandiyankha:Mundiphunzitse malemba anu.

27. Mundizindikiritse njira ya malangizo anu;Kuti ndilingalire zodabwiza zanu.

28. Moyo wanga wasungunuka ndi cisoni:Mundilimbitse monga mwa mau anu.

29. Mundicotsere njira ya cinyengo;Nimundipatse mwacifundo cilamulo canu.

30. Ndinasankha njira yokhulupirika;Ndinaika maweruzo anu pamaso, panga,

31. Ndimamatika nazo mboni zanu;Musandicititse manyazi, Yehova.

32. Ndidzathamangira njira ya malamulo anu,Mutakulitsa mtima wanga.

Masalmo 119