20. Mtima wanga wasweka ndi kukhumbaMaweruzo anu nyengo zonse.
21. Munadzudzula odzikuza otembereredwa,Iwo akusokera kusiyana nao malamulo anu.
22. Mundicotsere cotonza, ndi cimpepulo;Pakuti ndinasunga mboni zanu.
23. Nduna zomwe zinakhala zondineneza;Koma mtumiki wanu analingirira malemba anu.
24. Mboni zanu zomwe ndizo zondikondwetsa,Ndizo zondipangira nzeru.
25. Moyo wanga umamatika ndi pfumbi;Mundipatse moyo monga mwa mau anu.
26. Ndinafotokozera njira zanga, ndipo munandiyankha:Mundiphunzitse malemba anu.
27. Mundizindikiritse njira ya malangizo anu;Kuti ndilingalire zodabwiza zanu.
28. Moyo wanga wasungunuka ndi cisoni:Mundilimbitse monga mwa mau anu.
29. Mundicotsere njira ya cinyengo;Nimundipatse mwacifundo cilamulo canu.
30. Ndinasankha njira yokhulupirika;Ndinaika maweruzo anu pamaso, panga,
31. Ndimamatika nazo mboni zanu;Musandicititse manyazi, Yehova.
32. Ndidzathamangira njira ya malamulo anu,Mutakulitsa mtima wanga.
33. Mundiphunzitse, Yehova, njira ya malemba anu;Ndidzaisunga kufikira kutha kwace.
34. Mundizindikiritse, ndipo ndidzasunga malamulo anu;Ndidzawasamalira ndi mtima wanga wonse.
35. Mundiyendetse mopita malamulo anu;Pakuti ndikondwera m'menemo.
36. Lingitsani mtima wanga ku mboni zanu,Si ku cisiriro ai.
37. Mucititse mlubza maso anga ndisapenye zacabe,Mundipatse moyo mu njira yanu.
38. Limbitsirani mtumiki wanu mau anu,Ndiye wodzipereka kukuopani.