Masalmo 119:166-173 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

166. Ndinayembekeza cipulumutso canu, Yehova,Ndipo ndinacita malamulo anu.

167. Moyo wanga unasamalira mboni zanu;Ndipo ndizikonda kwambiri.

168. Ndinasamalira malangizo anu ndi mboni zanu;Popeza njira zanga zonse ziri pamaso panu,

169. Kupfuula kwanga kuyandikire pamaso pano, Yehova;Mundizindikiritse monga mwa mau anu.

170. Kupemba kwanga kudze pamaso panu;Mundilanditse monga mwa mau anu.

171. Milomo yanga iturutse cilemekezo;Popeza mundiphunzitsa malemba anu.

172. Lilime langa liyimbire mau anu;Pakuti malamulo anu onse ndiwo olungama.

173. Dzanja lanu likhale lakundithandizaPopezandinasankha malangizo anu.

Masalmo 119