165. Akukonda cilamulo canu ali nao mtendere wambiri;Ndipo alibe cokhumudwitsa.
166. Ndinayembekeza cipulumutso canu, Yehova,Ndipo ndinacita malamulo anu.
167. Moyo wanga unasamalira mboni zanu;Ndipo ndizikonda kwambiri.
168. Ndinasamalira malangizo anu ndi mboni zanu;Popeza njira zanga zonse ziri pamaso panu,
169. Kupfuula kwanga kuyandikire pamaso pano, Yehova;Mundizindikiritse monga mwa mau anu.
170. Kupemba kwanga kudze pamaso panu;Mundilanditse monga mwa mau anu.