Masalmo 119:163-167 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

163. Ndidana nalo bodza ndi kunyansidwa nalo;Koma ndikonda cilamulo canu.

164. Ndikulemekezani kasanu ndi kawiri, tsiku limodzi,Cifukwa ca maweruzo anu alungama.

165. Akukonda cilamulo canu ali nao mtendere wambiri;Ndipo alibe cokhumudwitsa.

166. Ndinayembekeza cipulumutso canu, Yehova,Ndipo ndinacita malamulo anu.

167. Moyo wanga unasamalira mboni zanu;Ndipo ndizikonda kwambiri.

Masalmo 119