163. Ndidana nalo bodza ndi kunyansidwa nalo;Koma ndikonda cilamulo canu.
164. Ndikulemekezani kasanu ndi kawiri, tsiku limodzi,Cifukwa ca maweruzo anu alungama.
165. Akukonda cilamulo canu ali nao mtendere wambiri;Ndipo alibe cokhumudwitsa.
166. Ndinayembekeza cipulumutso canu, Yehova,Ndipo ndinacita malamulo anu.
167. Moyo wanga unasamalira mboni zanu;Ndipo ndizikonda kwambiri.