Masalmo 119:160-168 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

160. Ciwerengero ca mau anu ndico coonadi;Ndi maweruzo anu olungama onse akhala kosatha.

161. Nduna zinandilondola kopanda cifukwa;Koma mtima wanga ucita mantha nao mau anu.

162. Ndikondwera nao mau anu,Ngati munthu wakupeza zofunkha zambiri.

163. Ndidana nalo bodza ndi kunyansidwa nalo;Koma ndikonda cilamulo canu.

164. Ndikulemekezani kasanu ndi kawiri, tsiku limodzi,Cifukwa ca maweruzo anu alungama.

165. Akukonda cilamulo canu ali nao mtendere wambiri;Ndipo alibe cokhumudwitsa.

166. Ndinayembekeza cipulumutso canu, Yehova,Ndipo ndinacita malamulo anu.

167. Moyo wanga unasamalira mboni zanu;Ndipo ndizikonda kwambiri.

168. Ndinasamalira malangizo anu ndi mboni zanu;Popeza njira zanga zonse ziri pamaso panu,

Masalmo 119