Masalmo 119:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndidzadzikondweretsa nao malemba anu;Sindidzaiwala mau anu,

17. Mucitire cokoma mtumiki wanu kuti ndikhale ndi moyo;Ndipo ndidzasamalira mau anu.

18. Munditsegulire maso, kuti ndipenyeZodabwiza za m'cilamulo canu.

19. Ine ndine mlendo pa dziko lapansi;Musandibisire malamulo anu.

Masalmo 119