159. Penyani kuti ndikonda malangizo anu;Mundipatse moyo, Yehova, monga mwa cifundo canu.
160. Ciwerengero ca mau anu ndico coonadi;Ndi maweruzo anu olungama onse akhala kosatha.
161. Nduna zinandilondola kopanda cifukwa;Koma mtima wanga ucita mantha nao mau anu.
162. Ndikondwera nao mau anu,Ngati munthu wakupeza zofunkha zambiri.
163. Ndidana nalo bodza ndi kunyansidwa nalo;Koma ndikonda cilamulo canu.