Masalmo 119:146-151 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

146. Ndinaitanira Inu; ndipulumutseni,Ndipo ndidzasamalira mboni zanu.

147. Ndinapfuula kusanace:Ndinayembekezera mau anu.

148. Maso anga anakumika malonda a usiku,Kuti ndilingirire mau anu.

149. Imvani liu langa monga mwa cifundo canu;Mundipatse moyo monga mwa kuweruza kwanu, Yehova.

150. Otsata zaciwembu andiyandikira;Akhala kutali ndi cilamulo canu.

151. Inu muli pafupi, Yehova;Ndipo malamulo anu onse ndiwo coonadi,

Masalmo 119