Masalmo 119:127-137 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

127. Cifukwa cace ndikonda malamulo anuKoposa golidi, Inde golidi woyengeka,

128. Cifukwa cace ndiyesa ngolunjika malangizo anu onse akunena zonse;Koma ndidana nazo njira zonse zonyenga.

129. Mboni zanu nzodabwiza; Cifukwa cace moyo wanga uzisunga,

130. Potsegulira mau anu paunikira;Kuzindikiritsa opusa.

131. Ndinatsegula pakamwa panga, ndi kupuma wefu wefu;Popeza ndinakhumba malamulo anu.

132. Munditembenukire, ndi kundicitira cifundo,Monga mumatero nao akukonda dzina lanu.

133. Kfiazikitsanimapaziangam'mau anu;Ndipo zisandigonjetse zopanda pace ziri zonse.

134. Mundiombole ku nsautso ya munthu:Ndipo ndidzasamalira malangizo anu.

135. Muwalitse nkhope yanu pa mtumiki wanu;Ndipo mundiphunzitse malemba anu.

136. Maso anga atsitsa mitsinje ya madzi,Popeza sasamalira cilamulo canu.

137. Inu ndinu wolungama, Yehova,Ndipo maweruzo anu ndiwo olunjika.

Masalmo 119