Masalmo 119:121-125 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

121. Ndinacita ciweruzo ndi cilungamo;Musandisiyira akundisautsa.

122. Mumkhalire cikole mtumiki wanucimkomere;Odzikuza asandisautse.

123. Maso anga anatha mphamvu pafuna cipulumutso canu,Ndi mau a cilungamo canu.

124. Mucitire mtumiki wanu monga mwa cifundo canu,Ndipo ndiphunzitseni malemba anu,

125. Ine ndine mtumiki wanu, ndizindikiritseni;Kuti ndidziwe mboni zanu.

Masalmo 119