Masalmo 119:113-121 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

113. Ndidana nao a mitima iwiri;Koma ndikonda cilamulo canu.

114. Inu ndinu pobisalapo panga, ndi cikopa canga;Ndiyembekezera mau anu.

115. Mundicokere ocita zoipa inu;Kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga.

116. Mundicirikize monga mwa mau anu, kuti ndikhale ndi moyo;Ndipo ndisacite manyazi pa ciyembekezo canga.

117. Mundigwirizize ndipo ndidzapulumutsidwa,Ndipo ndidzasamalira malemba anu cisamalire.

118. Mupepulaonseakusokeram'malemba anu;Popeza cinyengo cao ndi bodza.

119. Mucotsa oipa onse a pa dziko lapansi ngati mphala:Cifukwa cace ndikonda mboni zanu.

120. Thupi langa linjenjemera ndi kuopa Inu;Ndipo ndicita mantha nao maweruzo anu.

121. Ndinacita ciweruzo ndi cilungamo;Musandisiyira akundisautsa.

Masalmo 119