104. Malangizo anu andizindikiritsa;Cifukwa cace ndidana nao mayendedwe onse acinyengo,
105. Mau anu ndiwo nyali ya ku mapazi anga,Ndi kuunika kwa panjira panga,
106. Ndinalumbira, ndipo ndinatsimikiza mtima,Kuti ndidzasamalira maweruzo anu olungama.
107. Ndazunzika kwambiri:Ndipatseni moyo, Yehova, monga mwa mau anu.