Masalmo 118:7-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Yehova ndi wanga, mwa iwo akundithandiza;M'mwemo ndidzaona cofuna ine pa iwo akundida,

8. Kuthawira kwa Yehova nkokomaKoposa kukhulupirira munthu.

9. Kuthawira kwa Yehova nkokomaKoposa kukhulupirira akulu,

10. Amitundu onse adandizinga,Zedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.

11. Adandizinga, inde, adandizinga:Indedi, m'dzinala Yehova ndidzawaduladula.

12. Adandizinga ngati njuci;Anazima ngati moto waminga;Indedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.

13. Kundikankha anandikankha ndikadagwa;Koma Yehova anandithandiza.

14. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;Ndipo anakhala cipulumutso canga.

15. M'mahema a olungama muli liu lakupfuula mokondwera ndi la cipulumutso:

16. Dzanja lamanja la Yehova licita mwamphamvu.

17. Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo,Ndipo ndidzafotokozera nchito za Yehova.

18. Kulanga anandilangadi Yehova:Koma sanandipereka kuimfa ai.

19. Nditsegulireni zipata za cilungamo;Ndidzalowamo, ndidzayamika Yehova.

20. Cipata ca Yehova ndi ici;Olungama adzalowamo.

21. Ndidzakuyamikani, popeza munandiyankha,Ndipo munakhala cipulumutso canga,

22. Mwala umene omangawo anaukanaWakhala mutu wa pangondya.

23. Ici cidzera kwa Yehova;Ncodabwiza ici pamaso pathu.

24. Tsiku ili ndilo adaliika Yehova;Tidzasekera ndi kukondwera m'mwemo.

25. Tikupemphani, Yehova, tipulumutseni tsopano;Tikupemphani, Yehova, tipindulitseni tsopano.

26. Wodala wakudzayo m'dzina la Yehova;Takudalitsani kocokera m'nyumba ya Yehova.

Masalmo 118