Masalmo 118:12-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Adandizinga ngati njuci;Anazima ngati moto waminga;Indedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.

13. Kundikankha anandikankha ndikadagwa;Koma Yehova anandithandiza.

14. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;Ndipo anakhala cipulumutso canga.

15. M'mahema a olungama muli liu lakupfuula mokondwera ndi la cipulumutso:

16. Dzanja lamanja la Yehova licita mwamphamvu.

Masalmo 118