3. Zingwe za imfa zinandizinga,Ndi zowawa za manda zinandigwira:Ndinapeza nsautso ndi cisoni.
4. Pamenepo ndinaitana dzina la Yehova;Ndikuti, Yehova ndikupemphani landitsani moyo wanga.
5. Yehova ngwa cifundo ndi wolungama;Ndi Mulungu wathu ngwa nsoni.
6. Yehova asunga opusa;Ndidafoka ine, koma anandipulumutsa,