Masalmo 11:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Yehova ali m'Kacisi wace woyera,Yehova, mpando wacifumu wace uli m'Mwamba;Apenyerera ndi maso ace, ayesa ana a anthu ndi zikope zace.

5. Yehova ayesa wolungama mtima:Koma moyo wace umuda woipa ndi iye wakukonda ciwawa.

6. Adzagwetsa pwata pwata misampha pa oipa;Moto ndi miyala yasuifure, ndi mphepo yoopsa zidzawagawikira m'cikho cao.

7. Pakuti Yehova ndiye wolungama; akonda zolungama:Woongoka mtima adzapenya nkhope yace.

Masalmo 11