Masalmo 11:2-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Pakuti, onani, oipa akoka uta,Apiringidza mubvi wao pansinga,Kuwaponyera mumdima oongoka mtima.

3. Akapasuka maziko,Wolungama angacitenji?

4. Yehova ali m'Kacisi wace woyera,Yehova, mpando wacifumu wace uli m'Mwamba;Apenyerera ndi maso ace, ayesa ana a anthu ndi zikope zace.

5. Yehova ayesa wolungama mtima:Koma moyo wace umuda woipa ndi iye wakukonda ciwawa.

Masalmo 11