8. Ayamike Yehova cifukwa ca cifundo cace,Ndi zodabwiza zace za kwa ana a anthu!
9. Pakuti akhutitsa mtima wolakalaka,Nadzaza mtima wanjala ndi zabwino.
10. Iwo akukhala mumdima ndi mu mthunzi wa imfa,Omangika ndi kuzunzika ndi citsulo;
11. Popeza anapikisana nao mau a Mulungu,Napeputsa uphungu wa Wam'mwambamwamba;