Masalmo 107:33-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

33. Asanduliza mitsinje ikhale cipululu,Ndi akasupe a madzi akhale nthaka youma;

34. Dziko lazipatso, likhale lakhulo,Cifukwa ca coipa ca iwo okhalamo.

35. Asanduliza cipululu cikhale tha wale,Ndi dziko louma likhale akasupe a madzi.

36. Ndi apo akhalitsa anjala,Kuti amangeko mudzi wokhalamo anthu;

37. Nafese m'minda, naoke mipesa,Ndiyo vakubata zipatso zolemeza.

38. Ndipo awadalitsa, kotero kuti, acuruka kwambiri;Osacepsanso zoweta zao.

39. Koma acepanso, nawerama,Cifukwa ca cisautso, coipa ndi cisoni.

40. Atsanulira cimpepulo pa akulu,Nawasokeretsa m'cipululu mopanda njira.

Masalmo 107