Masalmo 107:28-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Pamenepo apfuulira kwa Yehova m'kusauka kwao,Ndipo awaturutsa m'kupsinjika kwao.

29. Asanduliza namondwe akhale bata,Kotero kuti mafunde ace atonthole.

30. Pamenepo akondwera, popeza pagwabata;Ndipo Iye awatsogolera kudooko afumko.

31. Ayamike Yehova cifukwa ca cifundo cace,Ndi zodabwiza zace za kwa ana a anthu!

32. Amkwezenso mu msonkhano wa anthu,Namlemekeze pokhala akulu.

33. Asanduliza mitsinje ikhale cipululu,Ndi akasupe a madzi akhale nthaka youma;

34. Dziko lazipatso, likhale lakhulo,Cifukwa ca coipa ca iwo okhalamo.

35. Asanduliza cipululu cikhale tha wale,Ndi dziko louma likhale akasupe a madzi.

Masalmo 107