Masalmo 107:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Anawaturutsa mumdima ndi mu mthunzi wa imfa,Nadula zomangira zao.

15. Ayamike Yehova cifukwa ca cifundo cace,Ndi zodabwiza zace za kwa ana a anthu!

16. Popeza adaswa zitseko zamkuwa,Natyola mipiringidzo yacitsulo.

17. Anthu opusa azunzika cifukwa ca zolakwa zao,Ndi cifukwa ca mphulupulu zao.

18. Mtima wao unyansidwa naco cakudya ciri conse;Ndipo ayandikira zipata za imfa.

19. Pamenepo apfuulira kwa Yehova m'kusauka kwao,Ndipo awapulumutsa m'kupsinjika kwao.

20. Atumiza mau ace nawaciritsa,Nawapulumutsa ku cionongeko cao.

Masalmo 107