Masalmo 105:37-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. Ndipo anawaturutsa pamodzi ndi siliva ndi golidi:Ndi mwa mafuko ao munalibe mmodzi wokhumudwa.

38. Aigupto anakondwera pakucoka iwo;Popeza kuopsa kwao kudawagwera.

39. Anayala mtambo uwaphimbe;Ndi moto uunikire usiku,

40. Anafunsa ndipo Iye anadzetsa zinziri.Nawakhuritsa mkate wakumwamba.

41. Anatsegula pathanthwe, anaturukamo madzi;Nayenda pouma ngati mtsinje.

42. Popeza anakumbukila mau ace oyera,Ndi Abrahamu mtumiki wace.

Masalmo 105