32. Anawapatsa mvula yamatalala,Lawi la moto m'dziko lao.
33. Ndipo anapanda mipesa yao, ndi mikuyu yao;Natyola mitengo kufikira m'malire ao onse.
34. Ananena, ndipo linadza dzombeNdi mphuci, ndizo zosawerengeka,
35. Ndipo zinadya zitsamba zonse za m'dziko mwao,Zinadyanso zipatso za m'nthaka mwao.