Masalmo 105:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yamikani Yehova, itanirani pa dzina lace;Bukitsani mwa mitundu ya anthu zocita Iye.

2. Myimbireni, myimbireni zomlemekeza;Fotokozerani zodabwiza zace zonse.

3. Mudzitamandire ndi dzina lace loyera:Mitima yao ya iwo ofunsira Yehova ikondwere.

4. Funani Yehova, ndi mphamvu yace;Funsirani nkhope yace nthawi zonse.

5. Kumbukilani zodabwiza zace adazicita;Zizindikilo zace ndi maweruzo a pakamwa pace;

Masalmo 105