17. M'mwemo mbalame zimanga zisa zao;Pokhala cumba mpa mitengo ya mikungudza,
18. Mapiri atali ndiwo ayenera zinkhoma;Pamatanthwe mpothawirapo mbira.
19. Anaika mwezi nyengo zace;Dzuwa lidziwa polowera pace.
20. Muika mdima ndipo pali usiku;Pamenepo zituruka zirombo zonse za m'thengo.