5. Amene akhutitsa m'kamwa mwako ndi zabwino;Nabweza ubwana wako unge mphungu.
6. Yehova acitira onse osautsidwa Cilungamo ndi ciweruzo.
7. Analangiza Mose njira zace,Ndi ana a Israyeli macitidwe ace.
8. Yehova ndiye wa nsoni zokoma ndi wacisomo,Wosakwiya msanga, ndi wa cifundo cocuruka.
9. Sadzatsutsana nao nthawi zanse;Ndipo sadzasunga mkwiyo wace kosatha.
10. Sanaticitira monga mwa zolakwa zathu,Kapena kutibwezera monga mwa mphulupulu zathu.