1. Ndipo anafika tsidya lina la nyanja, ku dziko la Agerasa,
2. Ndipo pameneadaturuka mungalawa, pomwepo anakomana naye munthu woturuka kumanda wa mzimu wonyansa,
3. amene anayesa nyumba yace kumanda; ndipo palibe munthu anakhoza kummanganso, inde ngakhale ndi unyolo;
4. pakuti adafomangidwa kawiri kawiri ndi matangadza ndimaunyolo, ndipo anamwetula maunyolo, naduladula matangadza; ndipo palibe munthu anali ndi mphamvu yakumfuya.