20. Ndipo anthu ambiri anasonkhananso, kotero kuti sanathe iwo konse kudya.
21. Ndipo pamene abale ace anamva, anadza kudzamgwira Iye; pakuti anati adayaruka.
22. Ndipo alembi amene adatsika ku Yerusalemu ananena kuti, Ali naye Beelzibule, ndipo, Ndi mkuru wao wa ziwanda aturutsa ziwanda.
23. Ndipo m'mene adawaitana iwo, ananena nao m'mafanizo, Satana angathe bwanji kuturutsa Satana?