19. ndi Yudase Isikariote, ndiye amene anampereka Iye.Ndipo analowa m'nyumba.
20. Ndipo anthu ambiri anasonkhananso, kotero kuti sanathe iwo konse kudya.
21. Ndipo pamene abale ace anamva, anadza kudzamgwira Iye; pakuti anati adayaruka.
22. Ndipo alembi amene adatsika ku Yerusalemu ananena kuti, Ali naye Beelzibule, ndipo, Ndi mkuru wao wa ziwanda aturutsa ziwanda.