Marko 14:56-60 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

56. Pakuti ambiri anamcitira umboni wonama, ndipo umboni wao sunalingana.

57. Ndipo ananyamukapo ena, namcitira umboni wakunama, nanena kuti,

58. Ife tinamva Iye alikunena, kuti, Ine ndidzaononga Kacisi uyu wopangidwa ndi manja, ndi masiku atatu ndidzamanga wina wosapangidwa ndi manja.

59. Ndipo ngakhale momwemo umboni wao sunalingana.

60. Ndipo mkulu wa ansembe ananyamuka pakati, namfunsa Yesu, nanena, Suyankha kanthu kodi? Nciani ici cimene awa alikucitira mboni?

Marko 14