29. Koma Petro ananena naye, Angakhale adzakhumudwa onse, komatu ine iai.
30. Ndipo Yesu ananena naye, Ndithu ndinena ndi iwe, kuti lero, usiku uno, tambala asanalire kawiri, udzandikana Ine katatu.
31. Koma iye analimbitsa mau cilimbitsire, kuti, Ngakhale ndidzafa nanu, sindidzakana Inu. Ndipo onsewo anatero.
32. Ndipo iwo anadza ku malo dzina lace Getsemane; ndipo ananena kwa ophunzira ace, Bakhalani pano, kufikira ndikapemphera.
33. Ndipo anatenga pamodzi ndi Iye Petro, ndi Yakobo, ndi Yohane, nayamba kudabwa kwambiri, ndi kusauka mtima ndithu.